
Bambo Isaac Phakala awamanga ku Chiradzulu powaganizila kuti analowelera mkangano wa m’banja mpaka kupha mwamuna yemwe anali mwini mkazi.
Malingana ndi Ofalitsa Nkhani za a Polisi m’bomali a Hubert Mwangoka, malemuwa amamenyana ndi mkazi wawo yemwe ndiwoyembekezera ndipo anamuvulaza kwambiri ndipo anamutengela kuchipatala.
Mwangoka wati atabwerako kuchipatalako woganiziridwayo anapita kunyumba komwe amakadzuzula malemuwo kuti asamamenye akazi awo. Izi akuti sizinasangalase malemuwo ndipo ndewu inayambika
Apa woganizilidwayu anatenga mpeni ndibaya nawo mwini mkaziyo pafupi ndi khutu.
Atathamanga nawo kuchipatala malemuwo anamwalira akulandira thandizo lachipatala.
A Phakala akuyembekezereka kukaonekela ku bwalo la milandu posachedwa kumene akayankhe mulando umene apalamulawu.



