
Confederation of African Football (CAF) yasankha woyimbira wa FIFA wa m’dziko la Ghana a Charles Bulu, kuti ndiye adzaimbire masewero oyamba a CAF Champions league pakati pa matimu Mighty Wanderers ndi Simba Sporting Club yaku Tanzania pa 6 September 2026 pa bwalo la Bingu mu mzinda wa Lilongwe.
CAF lasankhanso Seth Abletor komanso Richard Kweku Nartey ochokera ku Ghana komweko kuti ndi amene adzathandizire woyimbirayu.
Bungweli laika a Grema Mohammed aku Nigeria kuti adzagwire ntchito ngati oyimbira wapadera pamasewerowa
Matimu a Wanderers ndi Simba Sporting Club adzakumananso pamasewero achibwereza pa 12 September 2026 m’dziko la Tanzania.


