Screenshot
Zachitika dzuro zija ndizinthu zosakhara bwino mpang’ono pomwe kutsira utsi watsabola okhetsa misozi kwa Mtsogoleri wakale wa dziko. Ine mkuwona kwanga ndikuti amene muli pafupi ndi Dr Lazarus McCarthy Chakwera munapanga mistake yayikulu kulora kuti iwo atuluke mkukakhara nawo pa dipiti umene uja.
Ku MCP mukuyenera kuyamba ndiyinu kuteteza a Chakwera kuposa wina aliyese mdziko muno, mukuyenera kudziwa kuti iwowo ndi Pangolin wanu ndipo mbali inayo imawawopabe.
Mkanakhara kuti ine ndafusidwa maganizo anga mkanati Bwana asapite kumeneko, bwanawa panopo aloreni azipita ma ulendo awo akunja, koma osati public gatherings ngati ya dzuro ija. President amene watuluka kumene amakhara akuwopedwa mpaka next general election.
Tiyeni tipite ku 2014, Dr Joyce Banda ataluza chisankho anavomeleza ndipo anapita kukakhara ku Nkhatabay. Atakharakhara anatuluka mdziko muno ndipo posafuna kuti Boma lotsogozedwa ndi Prof Arthur Peter Mutharika liziti akuwasokoneza iwo anakhakhara kaye kunja.
A Peter Mutharika ataluza 2020, zomwe iwo anavomeleza mkukakhara ku PAGE House ku Mangochi. Iwo amkadziwa kuti Boma lomwe lapambana mposavuta kuwapezera milandu, chomcho iwo sanakhare busy kuwonekera ku dziko ndipo adayamba kulankhura patadutsa nthawi ndipo ankalankhulira kunyumba kwawo kudzera muma kalata kapena kuyitanitsa msonkhano wa tolankhani.
A Mutharika amkadziwa kuti pano alibeso mphavu ngati president ndipo a police omwe aja amkawalemekeza pano sangawapatseso ulemu ngati omwe uja. Iwo adadziyikira nthawi yozayamba kutuluka uko akuwona anyamata awo onse a kumangidwa ndipo amkadziwa kuti tchire lomwe lidstsara anali iwowo.
Kumbukirani kuti there is a difference between Power and Authority, munthu ungathe kukhara ndi mphavu koma ulamuliro ulibe. Mukamayenda pa nsewu mumatha kupeza wa traffic ka mtsikana kochepa nyama kungokweza dzanja inu kuyimitsa galimoto chufukwa ali ndi Authority, ka mnyamata kakang’ono kumanga chi bouncer cha mphavu that’s Authority, Wina ungathe kukhara wa dzimphavu kukayima pa nsewu koma Authority ulibe akuwombapo ndithu. Boma lilllonse loti lalowa kumene komaso zambiri sizikuyenda bwino silingalore kuti pakakhare ulendo wa ndawala ngati umene umachitika dzuro uja, chifukwa kuthekera koyamba mademo kumakhara pafupi kwambiri.
I repeat protect Dr Lazarus McCarthy Chakwera at all times, he is your Pangolin, nthawi ikwana yokha yoti ayambe kutuluka panopo azingolankhura ali kunyumba basi.