Mneneri wa chipani cha UTM Felix Njawala chipani cha MCP chinali ndi mwayi okonza magwiridwe a ntchito za a polisi mu zaka zisanu zomwe imalamulira.
Njawala walankhula izi pomwe ena otsatira chipanichi akudandaula ndi momwe apolisi agwirira ntchito yawo dzulo pomwe anathira utsi okhetsa msozi otsatira chipanichi.
Iwo akuti MCP inakanika kusintha momwe nthambi ya polisi imagwirira ntchito zake ndipo zimakanika kusiyanitsa polisi ndi chipani.
Njawala wati, “Munagula teargas wambiri kuposa chimanga cholinga muzitithila pazinthu zopanda pake. Munalanda ufulu wa anthu to demonstrate pomawathila teargas onse ofuna kupanga mademo.”
Iwo alemba izi pa tsamba lawo la mchezo kutsatira zomwe zinachitika dzulo.
Njawala wapitiliza kuti “Kuonjera pa teargas, munagulanso zikwanje nkumakhapa anthu police ndi army ili pompo osapanga kanthu.”
“Mudabwe kuti mmalo mokumverani chisoni anthu akusangalala. Muzigugude pa mtima panu ,muzilangize.” Anatero a Njawala.