
Anthu okwiya ku Chilipa m’boma la Mangochi awononga ma ofesi a Polisi ndi a Khoti kuderali posatila kusamvana komwe kunabuka pakayendesedwe ka mlandu wakusowa kwa mwana wina m’derali.
Amina Tepani Daudi wofalitsa nkhani za a Polisi m’bomali watsimikiza kuti nkhaniyi yachitika pa 25 August 2026 makolo ndi achibale amwana wosowayu atakhumudwa ndi kusakhutila ndi momwe nkhaniyi ikuyendera.
“Chinachitika ndi chakuti munthu yemwe akuganizilidwa kuti akukhuzidwa ndi kusowa kwa mwanayo amumasula ku Polisi ya Mangochi. Apa anthuwo anamemeza anzawo ndikuswa madzenela 8 ndi Chitseko pa Polisi ndi madzenela anayi pa Khothi ya Chilipa,” Watero Daudi.
Daudi wati a Polisi akhazikitsa kafukufuku kuti apeze ndi kumanga anthu amene achita izi.
Izi zachitika patangotha chaka chimodzi anthu enanso atawononga Polisi ya Katema yomwe ndiyoyandikana ndi Polisi ya Chilipa.



